×
Buku ili lasonkhanitsa kakhalidwe kwa amayi m’zipembedzo zitatu: Chiyuda, Chikristu ndi Chisilamu. Bukuli lalongosola mfundo zofunikira zochokera mu Chiyuda, komwe mzimayi sanangomutchula kuti ndi wochimwa, koma anatinso ndiyemwe anamuchimwitsa mwamuna. Koma Qur’an ili ndi kuwona kosiyana ndi mabuku ena onse, poti imamuona mzimai kuti ndi wofunikira kwambiri pa chitukuko cha munthu. Kumbali ya kuchimwa kapena kulungama, mzimai ali ndi kakhalidwe kofanana ndi mwamuna mchipembedzo; iye sichiyambi ya machismo onse. Bukuli lalongosola zokhudza Hijaab, ufulu wa kuphunzir kwa mkazi, ufulu wa kukhala ndi chuma chake pambuyo pa kukwatira, kulowa mmalo pambuyo pa kumwalira m’bale wake, mitala ndi nkhani zina. Awerengi a bukuli azindikira kusiyana komwe kulipo pakati pa Chisilamu ndi zipembedzo zina.